20 Ndipo taona, udzakhala wotonthola ndi wosakhoza kulankhula, kufikira tsiku limene zidzacitika izi, popeza kuti sunakhulupirira mau, anga, amene adzakwanitsidwa pa nyengo yace.
21 Ndipo anthu analikulindira Zakariya, nazizwa ndi kucedwa kwace m'kacisimo.
22 Koma m'mene iye anaturukamo, sanatha kulankhula nao; ndipo anazindikira kuti iye adaona masomphenya m'Kacisimo. Ndipo iye analinkukodola iwo, nakhalabe wosalankhula.
23 Ndipo kunali, pamene masiku a utumiki wace anamarizidwa, anamuka kunyumba kwace.
24 Ndipo atatha masiku awa, Elisabeti mkazi wace anaima; nadzibisa miyezi isanu, nati,
25 Ambuye wandicitira cotero m'masiku omwe iye anandipenyera, kucotsa manyazi anga pakati pa anthu.
26 Ndipo mwezi wacisanu ndi cimodzi mngelo Gabrieli anatumidwa ndi Mulungu kunka ku mudzi wa ku Galileya dzina lace N azarete,