4 kuti udziwitse zoona zace za mau amene unaphunzira.
5 Masiku a Herode, mfumu ya Yudeya, kunali munthu wansembe, dzina lace Zakariya, wa gulu la ansembe la Abiya; ndi mkazi wace wa ana akazi a pfuko la Aroni, dzina lace Elisabeti.
6 Ndipo onse awiri anali olungama mtima pamaso pa Mulungu, namayendabe m'malamulo onse ndi zoikika za Ambuye osacimwa.
7 Ndipo analibe mwana, popeza Elisabeti anali wouma, ndipo onse awiri anakalamba.
8 Ndipo panali, pakucita iye nchito yakupereka nsembe m'dongosolo la gulu lace, pamaso pa Mulungu, monga mwa macitidwe a kupereka nsembe,
9 adamgwera maere akufukiza zonunkhira polowa iye m'Kacisi wa Ambuye.
10 Ndipo khamu lonse la anthu Iinalikupemphera kunja nthawi ya zonunkhira.