39 Koma Ambuye anati kwa iye, Tsopano inu Afarisi muyeretsa kunja kwace kwa cikho ndi mbale, koma m'kati mwanu mudzala zolanda ndi zoipa.
40 Opusa inu, kodi iye wopanga kunja kwace sanapanganso m'kati mwace?
41 koma patsani mphatso yacifundo za m'katimo; ndipo onani, zonse ziri zoyera kwa inu.
42 Koma tsoka inu, Afarisi! cifukwa mupereka limodzi la magawo khumi la timbeu tonunkhira, ndi timbeu tokometsa cakudya ndi ndiwo zonse, ndipo mumaleka ciweruziro ndi cikondi ca Mulungu; mwenzi mutacita izi, ndi kusasiya zinazo.
43 Tsoka inu, Afarisi! cifukwa mukonda mipando yaulemu m'masunagoge, ndi kulankhulidwa m'misika.
44 Tsoka inu! cifukwa muli ngati manda osaoneka, ndipo anthu akuyendayenda pamwamba pao sadziwa,
45 Ndipo mmodzi wa acilamulo anayankha, nanena kwa iye, Mphunzitsi, ndi kunena izi, mutitonza ifenso.