15 Koma Ambuye anamyankha iye, nati, Onyenga inu, kodi munthu ali yense wa inu samaimasula ng'ombe yace, kapena buru wace kucodyeramo, tsiku la Sabata, kupita nayo kukaimwetsa madzi?
16 Ndipo mkazi uyu, ndiye mwana wa Abrahamu, amene Satana anammanga, onani, zaka khumi ndi zisanu ndi zitatu, nanga si kuyenera kodi, kuti amasulidwe nsinga yace imeneyi tsiku la Sabata?
17 Ndipo pamene Iye anatero, onse aja akutsutsana naye ananyazitsidwa; ndipo anthu onse a m'khamu anakondwera ndi zinthu zonse za ulemererozo zinacitidwa ndi iye.
18 Pamenepo ananena, Ufumu wa Mulungu ufanana ndi ciani? ndipo ndidzaufanizira ndi ciani?
19 Ufanana ndi kambeu kampiru, kamene munthu anatenga, nakaponya m'munda wace wace, ndipo kanamera, kanakula mtengo; ndi mbalame za m'mlengalenga zinabindikira mu nthambi zace.
20 Ndiponso anati, Ndidzafanizira Ufumu wa Mulungu ndi ciani?
21 Ufanana ndi cotupitsa mikate, cimene mkazianatenga, nacibisa mu miyeso itatu ya ufa, kufikira unatupa wonsewo,