22 Koma atateyo ananena kwaakapolo ace, Turutsani msanga mwinjiro wokometsetsa, nimumbveke; ndipo mpatseni phete ku dzanja lace ndi nsapato ku apazi ace;
23 ndipo idzani naye mwana wa ng'ombe wonenepa, mumuphe, ndipo tidye, tisekere;
24 cifukwa mwana wanga uyu anali wakufa, ndipo akhalanso wamoyo; anali wotayika, ndipo wapezedwa. Ndipo anayamba kusekera.
25 Koma mwana wace wamkuru anali kumunda. Ndipo pakubwera iye ndi kuyandikira kunyumba, anamva kuyimba ndi kubvina.
26 Ndipo anaitana mmodzi wa anayamata, namfunsa, Zinthu izi nzotani?
27 Ndipo uyu anati kwa iye, Mng'ono wako wafika; ndipo atate wako anapha mwana wa ng'ombe wonenepa, cifukwa anamlandira iye wamoyo.
28 Koma anakwiya, ndipo sanafuna kulowamo, Ndipo atate wace anaturuka namdandaulira.