3 Ndipo m'mudzimo munali mkazi wamasiye; ndipo anadza kwa iye nanena, Mundiweruzire mlandu pa wotsutsana nane.
4 Ndipo sanafuna nthawi; koma bwino bwino anati mwa yekha, Ndingakhale sindiopa Mulungu kapena kusamala munthu;
5 koma cifukwa ca kundibvuta ine mkazi wamasiye amene ndidzamweruzira mlandu, kuti angandilemetse ndi kudzaidza kwace.
6 Ndipo Ambuye anati, Tamverani conena woweruza wosalungama.
7 Ndipo kodi Mulungu sadzacitira cilungamo osankhidwa ace akumuitana usana ndi usiku, popeza aleza nao mtima?
8 Ndinena ndi inu, adzawacitira cilungamo posacedwa. Koma Mwana wa munthu pakudza Iye, vadzapeza cikhulupiriro pa dziko lapansi kodi?
9 Ndipo anatinso kwa ena amene anadzikhulupirira mwa iwo okha kuti ali olungama, napeputsa onse ena, fanizo ili,