27 Koma adani anga aja osafuna kuti ndidzakhala mfumu yao, bwerani cao kuno, nimuwaphe pamaso panga,
28 Ndipo m'mene adanena izi anawatsogolera nakwera ku Yerusalemu.
29 Ndipo kunali, m'mene anayandikira ku Betefage ndi Betaniya, pa phiri lochedwa la Azitona, anatuma awiri a ophunzira,
30 nati, Mukani ku mudzi uli pandunji panu; m'menemo, polowa, mudzapeza mwana wa buru womangidwa, pamenepo palibe munthu anakwerapo nthawi iri yonse; mummasule iye nimumtenge.
31 Ndipomunthuakati kwa inu, Mummasuliranji? mudzatero naye, Ambuye amfuna iye.
32 Ndipo anacoka otumidwawo, napeza monga adanena kwa iwo.
33 Ndipo pamene anamasula mwana wa buru, eni ace anati kwa iwo, Mumasuliranji mwana wa buru?