37 Pakuti ndinena ndi inu, cimene cidalembedwa ciyenera kukwanitsidwa mwa Ine, Ndipo anawerengedwa ndi anthu opanda lamulo; pakuti izi za kwa Ine ziri naco cimariziro.
38 Ndipo iwo anati, Ambuye, taonani, malupanga awir siwa. Ndipo anati kwa iwo, Cakwa nira.
39 Ndipo iye anaturuka, napita monga adafucita, ku phiri la Azitona ndi ophunzira anamtsata iye.
40 Ndipo pofika pomwepo, anati kwa iwo, Pempherani kuti mungalowe m'kuyesedwa.
41 Ndipo anapatukana nao kutalika kwace ngan kuponya mwala, nagwada pansi napemphera,
42 nati, Atate, mukafuna Inu, cotsani cikho ici pa Ine; koma si kufuna kwanga ai, komatu kwanu kucitike.
43 Ndipo anamuonekera iye 1 mngelo wa Kumwamba namlimbitsa iye.