31 Pakuti ngati azicitira izi mtengo wauwisi, nanga kudzatani ndi wouma?
32 Ndipo analinso awiri ena, ndiwo ocita zoipa; anatengedwa pamodzi ndi iye kuti aphedwe.
33 Ndipo pamene anafika ku malo dzina lace Bade, anampacika iye pamtanda pomwepo, ndi ocita zoipa omwe, mmodzi ku dzanja lamanja ndi wina kulamanzere.
34 Ndipo Yesu ananena, Atate, muwakhululukire iwo, pakuti sadziwa cimene acita. Ndipo anagawana zobvala zace, poyesa maere.
35 Ndipo anthu anaima alikupenya, Ndi akurunso anamlalatira iye nanena, Anapulumutsa ena; adzipulumutse yekha ngati iye ndiye Kristu wa Mulungu, wosankhidwa wace.
36 Ndipo asilikarinso anamnyoza, nadza kwa iye, nampatsa vinyo wosasa,
37 nanena, Ngati Iwe ndiwe Mfumu ya Ayuda, udzipulumutse wekha.