5 Koma iwo anapunda kunena kuti, Amautsa anthuwo, naphunzitsa m'Yudeya lonse, kuyambira ku Galileya ndi kufikira kuno komwe.
6 Koma pamene Pilato anamva, anafunsa ngati munthuyu ali Mgalileya.
7 Ndipo m'mene anadziwa kuti ali wa m'ulamuliro wace wa Herode, anamtumiza iye kwa Herode, amene anali iye mwini ku Yerusalemu masiku awa,
8 Ndipo Herode, pamene anaona Yesu, anakondwa ndithu; pakuti anayamba kale kufuna kumpenya iye, cifukwa anamva za iye; nayembekeza kuona cizindikilo cina cocitidwa ndi iye.
9 Ndipo anamfunsa iye mau ambiri; koma iye sanamyankha kanthu.
10 Ndipo ansembe akuru ndi alembi anaimirira, namnenera iye kolimba.
11 Ndipo Herode ndi asilikari ace anampeputsa iye, namnyoza, nambveka iye copfunda conyezimira, nambwezera kwa Pilato.