34 nanena, Ambuye anauka ndithu, naonekera kwa Simoni.
35 Ndipo iwo anawafotokozera za m'njira, ndi umo anadziwika nao m'kunyema kwa mkate.
36 Ndipo pakulankhula izi iwowa, iye anaimirira pakati pao; nanena nao, Mtendere ukhale nanu.
37 Koma anaopsedwandi kucita mantha, 1 nayesa alikuona mzimu.
38 Ndipo anati kwa iwo, Mukhala bwanji obvutika? ndipo matsutsano am auka bwanji m'mtima mwanu?
39 Penyani manja anga ndi mapazianga, kuti Ine ndine mwini: 2 ndikhudzeni, ndipo penyani; pakuti mzimu ulibe, mnofu ndi mafupa, monga muona ndirinazo Ine.
40 Ndipo m'mene ananena ici, anawaonetsera iwo manja ace ndi mapazi ace.