40 Ndipo m'mene ananena ici, anawaonetsera iwo manja ace ndi mapazi ace.
41 Koma pokhala iwo cikhalire osakhulupirira cifukwa ca cimwemwe, nalikuzizwa, anati kwa iwo, 3 Muli nako kanthu kakudya kuno?
42 Ndipo anampatsa iye cidutsu ca nsomba yokazinga.
43 Ndipo 4 anacitenga, nacidya pamaso pao.
44 Ndipo anati kwa iwo, 5 Awa ndi mauwo ndinalankhula nanu, paja ndinakhala ndi inu, kuti ziyenera kukwanitsidwa zonse zolembedwa za Ine m'cilamulo ca 6 Mose, ndi aneneri, ndi masalmo.
45 Ndipo 7 anawatsegulira mitima yao, kuti adziwitse malembo;
46 ndipo anati kwa iwo, 8 Kotero kwalembedwa, kuti Kristu amve zowawa, nauke kwa akufa tsiku lacitatu;