46 ndipo anati kwa iwo, 8 Kotero kwalembedwa, kuti Kristu amve zowawa, nauke kwa akufa tsiku lacitatu;
47 ndi kuti kulalikidwe m'dzina lace kulapa ndi 9 kukhululukidwa kwa macimo kwa 10 mitundu yonse, kuyambira ku Yerusalemu.
48 11 Inu ndinu mboni za izi.
49 Ndipo onani, 12 Ine nditumiza pa inu lonjezano la Atate wanga; koma khalani inu m'mudzi muno, kufikira mwabvekedwa ndi mphamvu yocokera Kumwamba.
50 Ndipo anaturuka nao kufikira ku Betaniya; nakweza manja ace, nawadalitsa.
51 Ndipo kunali, 13 pakuwadalitsa iye analekana nao, natengedwa kunka Kumwamba.
52 Ndipo 14 anamlambira iye, nabwera ku Yerusalemu ndi cimwemwe cacikuru;