6 Palibe kuno iye, komatu anauka; kumbukilani muja adalankhula nanu, pamene analinso m'Galileya,
7 ndi kunena, kuti, Mwana wa munthu ayenera kuperekedwa m'manja a anthu ocimwa, ndi kupacikidwa pamtanda, ndi kuuka tsiku lacitatu.
8 Ndipo anakumbukila mau ace, nabwera kucokera kumanda,
9 nafotokozera zonse khumi ndi mmodziwo, ndi otsala onse omwe.
10 Koma panali Mariya wa Magadala, ndi Y ohana, ndi Mariya amace wa Yakobo, ndi akazi ena pamodzi nao amene ananena izi kwa atumwiwo.
11 Ndipo mau awa anaoneka pamaso pao ngati nkhani zacabe, ndipo sanamvera akaziwo.
12 Koma Petro ananyamuka nathamangira kumanda, ndipo powerama anaona nsaru zoyera pa zokha; ndipo anacoka nanka kwao, nazizwa ndi cija cidacitikaco.