1 Ndipo Yesu, wodzala ndi Mzimu Woyera, anabwera kucokera ku Yordano, natsogozedwa ndi Mzimu kunka kucipululu kukayesedwa ndi mdierekezi masiku makumi anai.
2 Ndipo iye sanadya kanthu masiku awo; ndipo pamene anatha anamva njala.
3 Ndipo mdierekezi anati kwa iye, Ngati muli Mwana wa Mulungu, uzani mwala uwu usanduke mkate.
4 Ndipo Yesu anayankha nati kwa iye, Kwalembedwa, kuti,Munthu sadzakhala ndi moyo ndi mkate wokha.
5 Ndipo m'mene anamtsogolera anakwera naye, namuonetsa iye maufumu onse a dziko lokhalamo anthu, m'kamphindi kakang'ono.
6 Ndipo mdierekezi anati kwa iye, Ine ndidzapatsa Inu ulamuliro wonse umenewu ndi ulemerero wao: cifukwa unaperekedwa kwa ine; ndipo ndiupatsa kwa iye amene ndifuna.
7 Cifukwa cace ngati Inu mudzagwadira pamaso panga, wonsewo udzakhala wanu.