32 Ndipo panali pamenepo gulu la nkhumba zambiri zirinkudya m'phiri. Ndipo zinampempha Iye kuti azilole zilowe mu izo. Ndipo anazilola.
33 Ndipo ziwandazo zinaturuka mwa munthu nizilowa mu nkhumba: ndipo gululo linatsika liwiro potsetsereka ndi kulowa m'nyanjamo, nilitsamwa.
34 Ndipo akuwetawo m'mene anaona cimene cinacitika, anathawa, nauza a kumudzi ndi kumiraga yace.
35 Ndipo iwo anaturuka kukaona cimene cinacitika; ndipo anadza kwa Yesu, nampeza munthuyo, amene ziwanda zinaturuka mwa iye, alikukhala pansi ku mapazi ace a Yesu wobvala ndi wa nzeru zace; ndipo iwo anaopa.
36 Ndipo amene anaona anawauza iwo maciritsidwe ace a wogwidwa ciwandayo.
37 Ndipo anthu aunyinji onse a dziko la Agerasa Ioyandikira anamfunsa iye acoke kwa iwo; cifukwa anagwidwa ndi mantha akuru. Ndipo iye analowa m'ngalawa, nabwerera.
38 Ndipo munthuyo amene ziwanda zinaturuka mwa iye anampempha iye akhale ndi iye; koma anamuuza apite, nanena,