1 Ndipo iye anaitana pamodzi khumi ndi awiriwo nawapatsa mphamvu ndi ulamuliro pa ziwanda zonse, ndi zakuciritsa nthenda.
2 Ndipo anawatuma kukalalikira Ufumu wa Mulungu, ndi kuciritsa anthu odwala.
3 Ndipo iye anati kwa iwo, Musanyamule kanthu ka paulendo, kapena ndodo, kapena thumba, kapena mkate, kapena ndarama; ndipo musakhale nao malaya awiri.
4 Ndipo m'nyumba iri yonse mukalowemo, khalani komweko, ndipo muzikacokera kumeneko.