59 Ndipo anati kwa munthu wina, Unditsate Ine. Koma iye anati, Mundilole ine, Ambuye, ndithange ndamuka kuika maliro a atate wanga.
60 Koma anati kwa iye, Leka akufa aike akufa a eni okha; koma muka iwe nubukitse mbiri yace ya Ufumu wa Mulungu.
61 Ndipo winanso anati, Ambuye ndidzakutsatani Inu; koma muthange mwandilola kulawirana nao a kunyumba kwanga.
62 Koma Yesu anati kwa iye, Palibe munthu wakugwira cikhasu, nayang'ana za kumbuyo, ayenera Ufumu wa Mulungu.