5 Eluzai, ndi Yerimoti, ndi Bealiya, ndi Semariya, ndi Sefatiya wa ku Harupi,
6 Elikana, ndi Isiya, ndi Azereli, ndi Yoezeri, ndi Yasobeamu ndiwo Akora;
7 ndi Yoda, ndi Zebadiya, ana a Yerohamu wa ku Gedoro.
8 Ndi Agadi ena anapambukira kwa Davide ku liogala m'cipululu, ngwazi zamphamvu zozerewera nkhondo, zogwira cikopa ndi mkondo; nkhope zao zikunga nkhope za mikango, ndi liwiro lao longa la ngoma kumapiri:
9 Ezeri mkuru wao, waciwiri Obadiya, wacitatu Eliabu,
10 wacinai Misimana, wacisanu Yeremiya,
11 wacisanu ndi cimodzi Atai, wacisanu ndi ciwiri Elieli,