1 Mbiri 10 BL92

Za imfa ya Sauli ndi ana ace

1 Afilisti tsono analimbana nkhondo ndi Israyeli; ndipo amuna a Israyeli anathawa pamaso pa Afilisti, nagwa ophedwa pa phiri la Giliboa.

2 Ndipo Afilisti anaumirira kutsata Sauli ndi ana ace, ndi Afilistiwo anawapha Yonatani, ndi Abinadabu, ndi Malikisuwa, ana a Sauli.

3 Ndi nkhondoyi inamkulira Sauli, ndi amauta anampeza; ndipo anatenga nkhawa cifukwa ca amauta.

4 Pamenepo Sauli anati kwa wonyamula zida zace, Solola lupanga lako, nundipyoze nalo, angafike osadulidwa awa ndi kundiseka, Koma wonyamula zida zace anakana, popeza anaopa kwambiri. Pomwepo Sauli anatenga lupanga lace, naligwera.

5 Ndipo pamene wonyamula zida zace anaona kuti Sauli wafa, anagwera nayenso lupanga lace, nafa.

6 Momwemo anafa Sauli, ndi ana ace atatu; ndi nyumba yace yonse idafa pamodzi.

7 Ndipo pamene amuna onse a Israyeli okhala m'cigwamo anaona kuti anathawa, ndi kuti Sauli ndi ana ace adafa, anasiya midzi yao, nathawa; nadza Afilisti, nakhala m'menemo.

8 Ndipo m'mawa mwace anafika Afilisti kubvula za ophedwa, napeza Sauli ndi ana ace adagwa pa phiri la Giliboa.

9 Ndipo anambvula natenga mutu wace, ndi zida zace, natumiza ku dziko la Afilisti pozungulirapo, kulalika m'mafano ao ndi mwa anthu.

10 Ndipo anaika zida zace m'nyumba ya milungu yao, napacika mutu wace m'nyumba ya Dagoni.

11 Ndipo onse a Yabesi Gileadi, atamva zonse Afilisti adacitira Sauli,

12 anauka ngwazi zonse, nacotsa mtembo wa Sauli, ndi mitembo ya ana ace, nabwera nayo ku Yabesi, naika mafupa ao patsinde pa mtengo wathundu ku Yabesi, nasala masiku asanu ndi awiri.

13 Momwemo Sauli anafa, cifukwa ca kulakwa kwace analakwira Yehova, kulakwira mau a Yehova amene sanawasunga; ndiponso cifukwa ca kufunsira wobwebweta, kufunsirako,

14 osafunsira kwa Yehova; cifukwa cace anamupha, napambutsira ufumu kwa Davide mwana wa Jese.

Mitu

1 2 3 4 5 6 7 8 9 10 11 12 13 14 15 16 17 18 19 20 21 22 23 24 25 26 27 28 29