1 Mbiri 25 BL92

Cigawo ca oyimbira nyimbo

1 Ndipo Davide ndi akazembe a gulu la nkhondo anapatulira utumikiwo ena a ana a Asafu, ndi a Hemani, ndi a Yedutuni, anenere ndi azeze, ndi zisakasa, ndi nsanje; ndi ciwerengo ca anchito monga mwa kutumikira kwao ndko:

2 a ana a Asafu: Zakuri, ndi Yosefe, ndi Netaniya, ndi Asarela, ana a Asafu; mwa cilangizo ca Asafu, wakunenera mwa cilangizo ca mfumu.

3 A Yedntuni, ana a Yedutuni: Gedaliya, ndi Zeri, ndi Yesaya, Hasabiya, ndi Matitiya, asanu ndi mmodzi; mwa cilangizo ca atate wao Yedutuni, ndiye wakunenera ndi kuyamika ndi kulemekeza Yehova ndi zeze.

4 A Hemani, ana a Hemani: Bukiya, Mataniya, Uziyeli, Sebuyeli, ndi Yerimoti, Hananiya, Hanani, Eliyata, Gidaliti, ndi Romamti-Ezeri, Yosibekasa, Maloti, Hotiri, Mahazioti;

5 awa onse ndiwo ana a Hemani mlauli wa mfumu m'mau a Mulungu, kuti akweze mphamvu yace. Ndipo Mulungu anapatsa Hemani ana amuna khumi ndi anai, ndi ana akazi atatu.

6 Onsewa anawalangiza ndi atate wao ayimbe m'nyumba ya Yehova ndi nsanje, zisakasa ndi azeze; atumikire nazo m'nyumba ya Mulungu; ndipo Asafu, Yedutuni, ndi Hemani, anawalangiza ndi mfumu.

7 Ndipo ciwerengo cao, pamodzi ndi abale ao ophunzitsidwa ayimbire Yehova, onse anthetemya, ndiwo mazana awiri mphambu makumi asanu ndi atatu.

8 Ndipo anacita maere pa udikiro wao, analingana onse, ang'ono ndi akuru, mphunzitsi ndi wophunzira.

9 Maere oyamba tsono anagwera a banja la Asafu ndiye Yosefe; waciwiri Gedaliya, iye ndi abale ace, ndi ana ace khumi ndi awiri;

10 wacitatu Zakuri, ana ace ndi abale ace khumi ndi awiri;

11 wacinai Izri, ana ace ndi abale ace khumi ndi awiri;

12 wacisanu Netaniya, ana ace ndi abale ace khumi ndi awiri;

13 wacisanu ndi cimodzi Bukiya, ana ace ndi abale ace khumi ndi awiri;

14 wacisanu ndi ciwiri Yesarela: ana ace ndi abale ace khumi ndi awiri;

15 wacisanu ndi citatu Yesaya, ana ace ndi abale ace khumi ndi awiri;

16 wacisanu ndi cinai Mataniya, ana ace ndi abale ace khumi ndi awiri:

17 wakhumi Simeyi, ana ace ndi abale ace khumi ndi awiri;

18 wakhumi ndi cimodzi Azareli, ana ace ndi abale ace khumi ndi awiri;

19 wakhumi ndi ciwiri Hasabiya, ana ace ndi abale ace khumi ndi awiri;

20 wakhumi ndi citatu Subaeli, ana ace ndi abale ace khumi ndi awiri;

21 wakhumi ndi cinai Matitiya, ana ace ndi abale ace khumi ndi awiri;

22 wakhumi ndi cisanu Yeremoti, ana ace ndi abale ace khumi ndi awiri;

23 wakhumi ndi cisanu ndi cimodzi Hananiya, ana ace ndi abale ace khumi ndi awiri;

24 wakhumi ndi cisanu ndi ciwiri Yosibekasa, ana ace ndi abale ace khumi ndi awiri;

25 wakhumi ndi cisanu ndi citatu Hanani, ana ace ndi abale ace khumi ndi awiri;

26 wakhumi ndi cisanu ndi cinai Maloti, ana ace ndi abale ace khumi ndi awiri;

27 wa makumi awiri Eliyata, ana ace ndi abale ace khumi ndi awiri;

28 wa makumi awiri ndi cimodzi Hotiri, ana ace ndi abale ace khumi ndi awiri;

29 wa makumi awiri ndi ciwiri Gidaliti, ana ace ndi abale ace khumi ndi awiri;

30 wa makumi awiri ndi citatu Mahazioti, ana ace ndi abale ace khumi ndi awiri;

31 wa makumi awiri ndi cinai RomamtiEzeri, ana ace ndi abale ace khumi ndi awiri.

Mitu

1 2 3 4 5 6 7 8 9 10 11 12 13 14 15 16 17 18 19 20 21 22 23 24 25 26 27 28 29