1 Mbiri 3 BL92

Adzukulu a Davide

1 Ana Davide tsono ombadwira ku Hebroni: woyamba a Amnoni wa Ahinoamu wa ku Yezreeli, waciwiri Danieli wa Abigaili wa ku Karimeli,

2 wacitatu Abisalomu mwana wa Maaka mwana wamkazi wa Talimai mfumu ya Gesuri, wacinai Adoniya mwana wa Hagiti,

3 wacisanu Sefatiya wa Abitali, wacisanu ndi cimodzi Itreamu wa mkazi wace Egila,

4 Anambadwira asanu ndi mmodzi m'Hebroni; ndi pomwepo anakhala mfumu zaka zisanu ndi ziwiri, ndi miyezi isanu ndi iwiri; ndi m'Yerusalemu anakhala mfumu zaka makumi atatu mphambu zitatu.

5 Ndipo ombadwira m'Yerusalemu ndi awa: Simeya, ndi Sobabu, ndi Natani, ndi Solomo, anai a Batisuwa mwana wamkazi wa Amieli;

6 ndi Ibara, ndi Elisama, ndi Elifeleti,

7 ndi Noga, ndi Nefegi, ndi Yafiya,

8 ndi Elisama, ndi Eliada, ndi Elifeleti, asanu ndi anai.

9 Onsewa ndiwo ana a Davide, pamodzi ndi ana a akazi ang'ono; ndipo Tamara ndiye mlongo wao.

10 Ndipo mwana wa Solomo ndiye Rehabiamu, Abiya mwana wace, Asa mwana wace, Yeo hosafati mwana wace,

11 Yoramu mwana wace, Ahaziya mwana wace, Yoasi mwana wace,

12 Amaziya mwana wace, Azariya mwana wace, Yotamu mwana wace,

13 Ahazi mwana wace, Hezekiya mwana wace, Manase mwana wace,

14 Amoni mwana wace, Yosiya mwana wace.

15 Ndi ana a Yosiya: woyamba Yohanana, waciwiri Yehoyakimu, wacitatu Zedekiya, wacinai Salumu.

16 Ndi ana a Yehoyakimu: Yekoniya mwana wace, Zedekiya mwana wace.

17 Ndi mwana wa Yekoniya: Asiri, Sealitiyeli mwana wace,

18 ndi Malikiramu, ndi Pedaya, ndi Senazara, Yekamiya, Hosama, Nedabiya.

19 Ndi ana a Pedaya: Zerubabeli, ndi Simei; ndi ana a Zerubabeli: Mesulamu, ndi Hananiya; ndipo Selomiti ndiye mlongo wao,

20 ndi Hasuba, ndi Oheli, ndi Berekiya, ndi Hasadiya, ndi Yusabi-hesedi; asanu.

21 Ndi ana a Hananiya: Pelatiya, ndi Yesaya, ana a Refaya, ana a Arinani, ana a Obadiya, ana a Sekaniya.

22 Ndi mwana wa Sekaniya: Semaya; ndi ana a Semaya: Hatusi, ndi Igali, ndi Bariya, ndi Neariya, ndi Safati; asanu ndi mmodzi.

23 Ndi ana a Neariya: Eliunai, ndi Hizikiya, ndi Azrikamu, atatu.

24 Ndi ana a Eliunai: Hodavia, ndi Eliasibu, ndi Pelaya, ndi Akubu, ndi Yohanana, ndi Delaya, ndi Anani, asanu ndi awiri.

Mitu

1 2 3 4 5 6 7 8 9 10 11 12 13 14 15 16 17 18 19 20 21 22 23 24 25 26 27 28 29