4 Ndipo Davide anasonkhanitsa ana a Aroni ndi Alevi;
5 a ana a Kohati, Urieli mkuru wao, ndi abale ace zana limodzi mphambu makumi awiri;
6 a ana a Merari, Adaya mkuru wao, ndi abale ace mazana awiri mphambu makumi awiri;
7 a ana a Gerisomu, Yoeli mkuru wao, ndi abale ace zana limodzi mphambu makumi atatu;
8 a ana a Elizafana, Semaya mkuru wao, ndi abale ace mazana awiri;
9 a ana a Hebroni, Elieli mkuru wao, ndi abale ace makumi asanu ndi atatu;
10 a ana a Uzieli, Aminadabu mkuru wao, ndi abale ace zana limodzi mphambu khumi ndi awiri.