5 a ana a Kohati, Urieli mkuru wao, ndi abale ace zana limodzi mphambu makumi awiri;
6 a ana a Merari, Adaya mkuru wao, ndi abale ace mazana awiri mphambu makumi awiri;
7 a ana a Gerisomu, Yoeli mkuru wao, ndi abale ace zana limodzi mphambu makumi atatu;
8 a ana a Elizafana, Semaya mkuru wao, ndi abale ace mazana awiri;
9 a ana a Hebroni, Elieli mkuru wao, ndi abale ace makumi asanu ndi atatu;
10 a ana a Uzieli, Aminadabu mkuru wao, ndi abale ace zana limodzi mphambu khumi ndi awiri.
11 Ndipo anaitana Zadoki ndi Abyatara ansembe, ndi Alevi Urieli, Asaya, ndi Yoeli, Semaya, ndi Elieli, ndi Aminadabu, nanena nao,