13 Inu mbeu ya Israyeli mtumiki wace,Inu ana a Yakobo, osankhika ace.
14 Iye ndiye Yehova Mulungu wathu;Maweruzo ace akhala pa dziko lonse lapansi,
15 Kumbukilani cipangano cace kosatha,Mauwo anawalamulira mibadwo zikwi;
16 Cipanganoco anapangana ndi Abrahamu,Ndi lumbiro lace ndi Isake;
17 Ndipo anacitsimikizirakwa Yakobo cikhale malemba,Cikhale cipangano cosatha kwa Israyeli;
18 Ndi kunena kuti, Ndidzakupatsa iwe dziko la Kanani,Gawo la colandira cako;
19 Pokhala inu anthu owerengeka,Inde anthu pang'ono, ndi alendo m'mwemo;