16 Cipanganoco anapangana ndi Abrahamu,Ndi lumbiro lace ndi Isake;
17 Ndipo anacitsimikizirakwa Yakobo cikhale malemba,Cikhale cipangano cosatha kwa Israyeli;
18 Ndi kunena kuti, Ndidzakupatsa iwe dziko la Kanani,Gawo la colandira cako;
19 Pokhala inu anthu owerengeka,Inde anthu pang'ono, ndi alendo m'mwemo;
20 Nayendayenda kucokera mtundu wina kufikira mtundu wina,Kucokera ufumu wina kufikira anthu ena.
21 Sanalola munthu awasautse;Ndipo anadzudzula mafumu cifukwa ca iwowa;
22 Ndi kuti, Musamakhudza odzozedwa anga,Musamacitira coipa aneneri anga,