27 Ndipo Simei anali nao ana amuna khumi mphambu asanu ndi mmodzi, ndi ana akazi asanu ndi mmodzi; koma abale ace analibe ana ambiri, ndi banja lao lonse silinacurukitsa ngati ana a Yuda.
28 Ndipo anakhala ku Beereseba, ndi Molada, ndi Hazarasuala,
29 ndi ku Bila, ndi ku Ezemu, ndi ku Toladi,
30 ndi ku Betueli, ndi ku Horima, ndi ku Zikilaga,
31 ndi ku Betimarikaboti, ndi ku Hazarasusimu, ndi ku Betibiri, ndi ku Saraimu. Iyi ndi midzi yao, mpaka ufumu wa Davide, pamodzi ndi miraga yao.
32 Etamu, ndi Aini, Rimoni, ndi Tokeni, ndi Asani, midzi isanu;
33 ndi miraga yao yonse pozungulira pace pa midzi yomweyi, mpaka Baala. Apo ndi pokhala pao ndipo ali nao mawerengedwe a maina ao.