31 ndi ku Betimarikaboti, ndi ku Hazarasusimu, ndi ku Betibiri, ndi ku Saraimu. Iyi ndi midzi yao, mpaka ufumu wa Davide, pamodzi ndi miraga yao.
32 Etamu, ndi Aini, Rimoni, ndi Tokeni, ndi Asani, midzi isanu;
33 ndi miraga yao yonse pozungulira pace pa midzi yomweyi, mpaka Baala. Apo ndi pokhala pao ndipo ali nao mawerengedwe a maina ao.
34 Ndi Mesobabu, ndi Yamleki, ndi Yosa mwana wa Amaziya,
35 ndi Yoeli, ndi Yehu mwana wa Yosibiya, mwana wa Seraya, mwana wa Asieli;
36 ndi Eliunai, ndi Yaakoba, ndi Yesohaya, ndi Asaya, ndi Adieli, ndi Yesimieli, ndi Benaya,
37 ndi Ziza mwana wa Sifi, mwana wa Aloni, mwana wa Yedaya, mwana wa Simri, mwana wa Semaya;