33 ndi miraga yao yonse pozungulira pace pa midzi yomweyi, mpaka Baala. Apo ndi pokhala pao ndipo ali nao mawerengedwe a maina ao.
34 Ndi Mesobabu, ndi Yamleki, ndi Yosa mwana wa Amaziya,
35 ndi Yoeli, ndi Yehu mwana wa Yosibiya, mwana wa Seraya, mwana wa Asieli;
36 ndi Eliunai, ndi Yaakoba, ndi Yesohaya, ndi Asaya, ndi Adieli, ndi Yesimieli, ndi Benaya,
37 ndi Ziza mwana wa Sifi, mwana wa Aloni, mwana wa Yedaya, mwana wa Simri, mwana wa Semaya;
38 awa ochedwa maina ndiwo akalonga m'mabanja ao, ndi nyumba za makolo ao zinacuruka kwambiri.
39 Ndipo anamuka mpaka polowera ku Gedoro kum'mawa kwa cigwa, kufunafuna podyetsa zoweta zao.