4 ndi Penueli atate wa Gedoro, ndi Ezeri atate wa Husa. Awa ndi ana a Huri woyamba wa Efrata atate wa Betelehemu.
5 Ndipo Asuri atate wa Tekowa anali nao akazi awiri: Hela, ndi Naara.
6 Ndi Naara anambalira Ahuzamu, ndi Heferi, ndi Temeni, ndi Hahastario Iwo ndiwo ana a Naara.
7 Ndi ana a Hela ndiwo Zereti, lzara, ndi Etinani.
8 Ndipo Hakozi anabala Anubu, ndi Zobeba, ndi mabanja a Ahareli mwana wa Harumu.
9 Ndipo Yabezi analemekezedwa koposa abale ace; ndi mace anamucha dzina lace Yabezi, ndi kuti, Popeza ndambala mwaululu.
10 Ndipo Yabezi anaitana kwa Mulungu wa Israyeli, ndi kuti, Mundidalitse ndithu, ndi kukulitsa malire anga; ndi dzanja lanu likhale ndi ine, nimundisunge, kuti coipa cisandibvute. Ndipo Mulungu anafikitsa copempha iye.