9 Ndipo Yabezi analemekezedwa koposa abale ace; ndi mace anamucha dzina lace Yabezi, ndi kuti, Popeza ndambala mwaululu.
10 Ndipo Yabezi anaitana kwa Mulungu wa Israyeli, ndi kuti, Mundidalitse ndithu, ndi kukulitsa malire anga; ndi dzanja lanu likhale ndi ine, nimundisunge, kuti coipa cisandibvute. Ndipo Mulungu anafikitsa copempha iye.
11 Ndipo Kelubu mbale wa Sua anabala Mehiri, ndiye atate wa Esitoni.
12 Ndi Esitoni anabala Betirafa, ndi Paseya, ndi Tehina atate wa Irinahasi. Awa ndi anthu a Reka.
13 Ndi ana a Kenazi: Otiniyeli, ndi Seraya; ndi mwana wa Otmiyeh: Hatati.
14 Ndipo Meonotai anabala Ofra; ndi Seraya anabala Yoabu atate wa Geharasimu; popeza iwo ndiwo amisiri.
15 Ndi ana a Kalebi mwana wa Yefune: Iru, Ela, ndi Naamu; ndi ana a Ela, ndi Kenazi.