1 Ndipo ana a Rubeni mwana woyamba wa Israyeli, (pakuti ndiye mwana woyamba; koma popeza anaipsa kama wa atate wace ukulu wace unapatsidwa kwa ana a Yosefe mwana wa Israyeli, koma m'buku la cibadwidwe asayesedwe monga mwa ukulu wace.
2 Pakuti Yuda anakula mphamvu mwa abale ace, ndi mtsogoleri anafuma kwa iyeyu, koma ukulu ngwa Yosefe);
3 ana a Rubeni mwana woyamba wa Israyeli: Hanoki, ndi Palu, Hezroni, ndi Karmi.
4 Ana a Yoeli: Semaya mwana wace, Gogi mwana wace, Simei mwana wace,
5 Mika mwana wace, Reaya mwana wace, Baala mwana wace,
6 Beera mwana wace, amene Tigilati Pilesere wa ku Asuri anamtenga ndende; ndiye kalonga wa Arubeni.
7 Ndi abale ace monga mwa mabanja ao, powerenga cibadwidwe ca mibadwo yao: akuru ndiwo Yeyeli, ndi Zekariya,