3 Ndipo m'Yerusalemu munakhala a ana a Yuda, ndi a ana a Benjamini, ndi a ana a Efraimu ndi Manase:
4 Utai mwana wa Amihudi, mwana wa Omri, mwana wa Imri, mwana wa Bani, wa ana a Perezi mwana wa Yuda.
5 Ndipo a Asiloni: Asaya woyamba, ndi ana ace.
6 Ndi a ana a Zera: Yeueli ndi abale ao mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi asanu ndi anai.
7 Ndi a ana a Benjamini: Salu mwana wa Mesulamu, mwana wa Hodavia, mwana wa Hasenuwa;
8 ndi Ibineya mwana wa Yerohamu, ndi Ela mwana wa Uzi, mwana-wa Mikiri, ndi Mesulamu mwana wa Sefatiya, mwana wa Reueli, mwana wa Ibniya,
9 ndi abale ao monga mwa mibadwo yao mazana asanu ndi anai mphambu makumi asanu kudza asanu ndi mmodzi. Onsewa ndiwo akuru a nyumba za makolo ao m'nyumba za makolo ao.