9 Adzasunga mapazi a okoodedwaace,Koma oipawo adzawakhalitsa cete mumdima;Pakuti palibe munthu adzapambana ndi mphamvu,
10 Otsutsana ndi Yehova adzaphwanyika;Kumwamba iye adzagunda pa iwo:Yehova adzaweruza malekezero a dziko:Ndipo adzapatsa mphamvu mfumuyace,Nadzakweza nyanga ya wodzozedwa wace.
11 Ndipo Elikana anauka kwao ku Rama, mwanayo natumikira Yehova pamaso pa Eli wansembeyo.
12 Koma ana a Eli anali oipa; sanadziwa Yehova.
13 Ndipo macitidwe a ansembe akucitira anthu ndiwo, kuti pamene munthu ali yense akapereka nsembe, mnyamata wa wansembeyo akabwera, nyama iri ciwirire, ndi cobvuulira ca ngowe ca mana atatu m'dzanja lace;
14 nacipisa m'cimphuli, kapena mumkhate, kapena m'nkhali, kapena mumphika; yonse imene cobvuuliraco cinaiturutsa, wansembeyo anaitenga ikhale yace. Adafotero ku Silo ndi Aisrayeli onse akufika kumeneko.
15 Ngakhale asanayambe kupsereza mafuta, amadza mnyamata wa wansembe, namuuza wopereka nsembe, nati, Umpatse wansembeyo nyama yoti akaoce; pakuti safuna nyama yako yophika koma yaiwisi.