10 Ndipo anaika zida zace m'nyumba ya Asitarote; napacika mtembo wace ku linga la ku Betisani.
11 Koma pamene a ku Jabezi Gileadi anamva zimene Afilisti anamcitira Sauli,
12 ngwazi zonse zinanyamuka ndi kucezera usiku kuyenda, natenga mtembo wa Sauli, ndi mitembo ya ana ace, pa linga la Betisani; nafika ku Jabezi Gileadi naitentha kumeneko.
13 Natenga mafupa ao nawaika patsinde pa mtengo uli m'Jabezi, nasala kudya masiku asanu ndi awiri.