16 Nagona Yoasi ndi makolo ace, namuika m'Samariya pamodzi ndi mafumu a Israyeli; nakhala mfumu m'malo mwace Yerobiamu mwana wace.
17 Ndipo Amaziya mwana wa Yoasi mfumu ya Yuda anakhala ndi moyo, atamwalira Yoasi mwana wa Yoahazi mfumu ya Israyeli, zaka khumi ndi zisanu.
18 Macitidwe ena tsono a Amaziya, kodi sizilembedwa m'buku la macitidwe a mafumu a Yuda?
19 Ndipo anamcitira ciwembu m'Yerusalemu, nathawira iye ku Lakisi; koma anatumiza akumtsata ku Lakisi, namupha komweko.
20 Nabwera naye pa akavalo, namuika ku Yerusalemu pamodzi ndi makolo ace m'mudzi wa Davide.
21 Ndipo anthu onse a Yuda anatenga Azariya, (ndiye Uziya), ndiye wa zaka khumi mphambu zisanu ndi cimodzi, namlonga ufumu m'malo mwa atate wace Amaziya,
22 Anamanga Elati, naubweza kwa Yuda, atagona ndi makolo ace mfumuyo.