5 Ndipo kunali, utakhazikika ufumu m'dzanja lace, anakantha anyamata ace amene adakantha mfumu atate wace;
6 koma ana a ambandawo sanawapha, monga mwalembedwa m'buku la cilamulo ca Mose, m'mene adalamulira Yehova, ndi kuti, Atate asaphedwere ana, kapena ana kuphedwera atate; koma yense afere kulak wa kwa iye yekha.
7 Anapha Aedomu m'Cigwa ca Mcere zikwi khumi, nalanda Sela ndi nkhondo, naucha dzina lace Yokiteli mpaka lero lino.
8 Pamenepo Amaziya anatuma mithenga kwa Yoasi mwana wa Yoahazi mwana wa Yehu mfumu ya Israyeli, ndi kuti, Idzani tionane maso.
9 Natumiza Yoasi mfumu ya Israyeli kwa Amaziya mfumu ya Yuda, ndi kuti, Mtungwi wa ku Lebano unatumiza mau kwa mkungudza wa ku Lebano, ndi kuti, Mpatse mwana wanga wamwamuna mwana wako wamkazi akhale mkazi wace; ndipo Inapitapo nyama ya kuthengo ya ku Lebano, nipondereza mtungwiwo.
10 Wakanthadi Aedomu, koma mtima wako wakukweza; ulemekezeke, nukhale kwanu; udziutsiranji tsoka, ungagwe iwe ndi Yuda pamodzi nawe;
11 Koma Amaziya sanamvera. Motero anakwera Yoasi mfumu ya Israyeli, ndipo iye ndi Amaziya mfumu ya Yuda anapenyana maso ku Betisemesi, ndiwo wa Yuda.