9 Namuka Hazaeli kukakomana naye, napita naco caufulu, ndico ca zokoma zonse za m'Damasiko, zosenza ngamila makumi anai, nafika naima pamaso pace, nati, Mwana wanu Benihadadi mfumu ya Aramu, wandituma ine kwa inu, ndi kuti, Kodi ndidzacira nthenda iyi?
10 Nanena naye Elisa, Kamuuze, kuti, Sudzacira konse; popeza Yehova wandionetsa kuti adzafa ndithu.
11 Ndipo anamyang'ana cidwi, mpaka anacita manyazi, nalira misozi munthu wa Mulungu.
12 Nati Hazaeli, Muliriranji, mbuye wanga? Nayankha iye, Popeza ndidziwa coipa udzacitira ana a Israyeli; udzatentha malinga ao ndi moto, nudzapha anyamata ao ndi lupanga, nudzaphwanya makanda ao, nudzang'amba akazi ao okhala ndi pakati.
13 Nati Hazaeli, Koma nanga kapolo wanu ali ciani, ndiye garu, kuti akacite cinthu cacikuru ici? Nayankha Elisa, Yehova wandionetsa kuti udzakhala mfumu ya pa Aramu.
14 Ndipo anacoka kwa Elisa, nadza kwa mbuye wace; ameneyo ananena naye, Anakuuza ciani Elisa? Nati iye, Anandiuza kuti mudzacira ndithu.
15 Ndipo kunali m'mawa mwace, anatenga cimbwi, nacibviika m'madzi, naciphimba pankhope pa mfumu, nifa; ndipo Hazaeli analowa ufumu m'malo mwace.