10 Ndipo khamu lonse la anthu Iinalikupemphera kunja nthawi ya zonunkhira.
11 Ndipo anamuonekera iye mngelo wa Ambuye, naimirira ku dzanja lamanja la guwa la nsembe la zonunkhira.
12 Ndipo Zakariya anadabwa pamene anamuona, ndipo mantha anamgwira.
13 Koma mngelo anati kwa iye, Usaope Zakariya, cifukwa kuti lamveka pemphero lako, ndipo mkazi wako adzakubalira mwana wamwamuna, ndipo udzamucha dzina lace Yohane.
14 Ndipo udzakhala nako kukondwera ndi msangalalo; ndipo anthu ambiri adzakondwera pa kubadwa kwace.
15 Pakuti iye adzakhala wamkuru pamaso pa Ambuye, ndipo sadzamwa konse vinyo kapena, kacasu; nadzadzazidwa ndi Mzimu Woyera, kuyambira asanabadwe.
16 Ndipo iye adzatembenuzira ana a Israyeli ambiri kwa Ambuye Mulungu wao.