7 Ndipo tsiku la mikate yopanda cotupitsa linafika, limene inayenera kuphedwa nsembe ya Paskha.
8 Ndipo iye anatumiza Petro ndi Yohane, nati, Pitanimutikonzere ife Paskha, kuti tidye.
9 Ndipo iwo ananena naye, Mufuna tikakonzere kuti?
10 Ndipo iye anati kwa iwo, Onani, mutalowa m'mudzi, adzakomana ndinu munthu alikusenza mtsuko wa madzi; mumtsate ameneyo kunyumba kumene akalowako iye.
11 Ndipo mukanene kwa mwini nyumbayo, Mphunzitsi anena nawe, Cipinda ca alendo ciri kuti, m'mene ndikadye Paskha pamodzi ndi ophunzira anga?
12 Ndipo iyeyo adzakuonetsani cipinda cacikuru capamwamba, cokonzeka; mukakonzere kumeneko.
13 Ndipo anapita iwo, napeza monga adatero nao; ndipo anakonza Paskha.