19 ndiye munthu anaponyedwa m'ndende cifukwa ca mpanduko m'mudzi ndi ca kupha munthu.
20 Ndipo Pilato analankhulanso nao, nafuna kumasula Yesu;
21 koma iwo anapfuula, nanena, Mpacikeni, mpacikeni pamtanda.
22 Ndipo anati kwa iwo nthawi yacitatu, Nanga munthuyu anacita coipa ciani? Sindinapeza cifukwa ca kufera iye; cotero ndidzamkwapula iye ndi kummasula.
23 Koma anakakamiza ndi mau okweza, napempha kuti iye apacikidwe, Ndipo mau ao analakika.
24 Ndipo Pilato anaweruza kuti cimene alikufunsa cicitidwe.
25 Ndipo anawamasulira amene adaponyedwa m'ndende cifukwa ca mpanduko ndi kupha munthu, amene iwo anampempha; koma anapereka Yesu mwa cifuniro cao.