27 Uyu ndi iye amene kunalembedwa za iye,Ona, ndituma Ine mthenga wanga akutsogolere,Amene adzakukonzera njira yako pamaso pako.
28 Ndinena kwa inu, kuti, Mwa akubadwa ndi akazi palibe mmodzi wamkuru woposa Yohane; koma iye amene ali wamng'ono mu Ufumu wa Mulungu amposa iye.
29 Ndipo anthu onse ndi amisonkho omwe, pakumva, anabvomereza kuti Mulungu ali wolungama, popeza anabatizidwa iwo ndi ubatizo wa Yohane.
30 Koma Afarisi ndi acilamulo anakaniza uphungu wa Mulungu kwa iwo okha, popeza sanabatizidwa ndi iye.
31 Ndipo, ndidzafanizira ndi ciani anthu a mbadwo uno? ndipo afanana ndi ciani?
32 Angofanana ndi ana akukhala pamsika, ndi kuitanizana wina ndi mnzace, ndi kunena, Ife tinakulizirani citoliro, ndipo inu simunabvina ai; tinabuma maliro, ndimo simunalira ai.
33 Pakuti Yohane Mbatizi wafika wosadya mkate ndi wosamwa vinyo; ndipo munena, Ali ndi ciwanda.