5 Anaturuka wofesa kukafesa mbeu zace; ndipo m'kufesa kwace zina zinagwa m'mbali mwa njira; ndipo zinapondedwa, ndi mbalame za m'mlengalenga zinatha kuzidya.
6 Ndipo zina zinagwa pathanthwe; ndipo pakumera zinatofa msanga, cifukwa zinalibe mnyontho.
7 Ndipo zina zinagwa pakati pa minga; ndi mingayo inapuka pamodzi nazo, nizitsamwitsa.
8 Ndipo zina zinagwa pa nthaka yokoma, ndipo zinamera, ndi kupatsa zipatso zamakumikhumi. Pakunena iye izi anapfuula, iye amene ali ndi makutu akumva amve.
9 Ndipo ophunzira ace anamfunsa Iye, kuti, Fanizo ili liri lotani?
10 Ndipo iye anati, Kwapatsidwa kwa inu kuzindikira zinsinsi za Ufumu wa Mulungu; koma kwa ena otsala ndinena nao mwa mafanizo; kuti pakuona sangaone, ndi pakumva sangadziwitse,
11 Koma fanizoli litere: Mbeuzo ndizo mau a Mulungu,