7 Ndipo zina zinagwa pakati pa minga; ndi mingayo inapuka pamodzi nazo, nizitsamwitsa.
8 Ndipo zina zinagwa pa nthaka yokoma, ndipo zinamera, ndi kupatsa zipatso zamakumikhumi. Pakunena iye izi anapfuula, iye amene ali ndi makutu akumva amve.
9 Ndipo ophunzira ace anamfunsa Iye, kuti, Fanizo ili liri lotani?
10 Ndipo iye anati, Kwapatsidwa kwa inu kuzindikira zinsinsi za Ufumu wa Mulungu; koma kwa ena otsala ndinena nao mwa mafanizo; kuti pakuona sangaone, ndi pakumva sangadziwitse,
11 Koma fanizoli litere: Mbeuzo ndizo mau a Mulungu,
12 Ndipo za m'mbali mwa njira ndiwo anthu amene adamva; pamenepo akudza mdierekezi, nacotsa mau m'mitima yao, kuti angakhulupirire ndi kupulumuka.
13 Ndipo za pathanthwe ndiwo amene, pakumva, alandira mau ndi kukondwera; koma alibe mizu; akhulupirira kanthawi, ndipo pa nthawi ya mayesedwe angopatuka.