8 Ndi Agadi ena anapambukira kwa Davide ku liogala m'cipululu, ngwazi zamphamvu zozerewera nkhondo, zogwira cikopa ndi mkondo; nkhope zao zikunga nkhope za mikango, ndi liwiro lao longa la ngoma kumapiri:
9 Ezeri mkuru wao, waciwiri Obadiya, wacitatu Eliabu,
10 wacinai Misimana, wacisanu Yeremiya,
11 wacisanu ndi cimodzi Atai, wacisanu ndi ciwiri Elieli,
12 wacisanu ndi citatu Yohanani, wacisanu ndi cinai Elzabadi,
13 wakhumi Yeremiya, wakhumi ndi cimodzi Makibanai.
14 Awa a ana a Gadi, anali atsogoleri a nkhondo; wamng'ono wa iwo anayang'anira zana limodzi, ndi wamkuru wa iwo anayang'anira cikwi cimodzi.