7 a ana a Gerisomu, Yoeli mkuru wao, ndi abale ace zana limodzi mphambu makumi atatu;
8 a ana a Elizafana, Semaya mkuru wao, ndi abale ace mazana awiri;
9 a ana a Hebroni, Elieli mkuru wao, ndi abale ace makumi asanu ndi atatu;
10 a ana a Uzieli, Aminadabu mkuru wao, ndi abale ace zana limodzi mphambu khumi ndi awiri.
11 Ndipo anaitana Zadoki ndi Abyatara ansembe, ndi Alevi Urieli, Asaya, ndi Yoeli, Semaya, ndi Elieli, ndi Aminadabu, nanena nao,
12 Inu ndinu akuru a nyumba za makolo a Alevi, mudzipatule inu ndi abale anu omwe, kuti mukatenge ndi kukwera nalo likasa la Yehova Mulungu wa Israyeli ku malo ndalikonzera.
13 Pakuti, cifukwa ca kusalinyamula inu poyamba paja, Yehova Mulungu wathu anacita cotipasula, popeza sitinamfunafuma Iye monga mwa ciweruzo.