1 Ndipo pokhala Davide m'nyumba mwace, Davideyo anati kwa Natani mneneri, Taona, ndikhala ine m'nyumba yamikungudza, koma Gkasa la cipangano likhala m'nsaru zocinga.
2 Ndipo Natani anati kwa Davide, Mucite zonse ziri m'mtima mwanu; pakuti Mulungu ali nanu.
3 Ndipo usiku womwewo mau a Mulungu anadzera Natani, ndi kuti,
4 Kauze Davide mtumiki wanga, Atero Yehova, Usandimangire nyumba yokhalamo;