14 Kunena za Mose munthu wa Mulunguyo, ana ace anaehulidwa mwa pfuko la Levi.
15 Ana a Mose: Gerisomu, ndi Eliezeri.
16 Ana a Gerisomu: wamkuru ndi Sebuyeli.
17 Ndi ana a Eliezeri: wamkuru ndi Rehabiya. Ndipo Eliezeri analibe ana ena, koma ana a Rehabiya anacuruka kwambiri.
18 Ana a Izara: wamkuru ndiye Selomiti.
19 Ana a Hebroni: wamkuru ndi Yeriya, waciwiri ndi Amariya, wacitatu ndi Yehazieli, wacinai ndi Yekameamu,
20 Ana a Uzieli: wamkuru ndi Mika, waciwiri ndi Isiya.