16 Ana a Gerisomu: wamkuru ndi Sebuyeli.
17 Ndi ana a Eliezeri: wamkuru ndi Rehabiya. Ndipo Eliezeri analibe ana ena, koma ana a Rehabiya anacuruka kwambiri.
18 Ana a Izara: wamkuru ndiye Selomiti.
19 Ana a Hebroni: wamkuru ndi Yeriya, waciwiri ndi Amariya, wacitatu ndi Yehazieli, wacinai ndi Yekameamu,
20 Ana a Uzieli: wamkuru ndi Mika, waciwiri ndi Isiya.
21 Ana a Merari: Mali ndi Musi. Ndi ana a Mali: Eleazara ndi Kisi.
22 Nafa Eleazara wopanda ana amuna, koma ana akazi ndiwo; ndi asuweni ao ana a Kisi anawatenga akhale akazi ao.