19 Awa ndi malongosoledwe ao m'utumiki wao kulowa m'nyumba ya Yehova, monga mwa ciweruzo adawapatsa Aroni atate wao, monga Yehova Mulungu wa Israyeli anamlamulira.
20 Ndipo wa ana otsala a Levi: wa ana a Amiramu, Subaeli; wa ana a Subaeli, Yedeya.
21 Wa Rehabiya: wa ana a Rehabiya, mkuru ndi Isiya.
22 Wa Aizari: Selomoti; wa ana a Selomoti, Yahati.
23 Ndi wa ana a Hebroni: mkuru ndi Yeriya, waciwiri Amariya, wacitatu Yahazieli, wacinai Yekameamu.
24 Wa ana a Uziyeli, Mika; wa ana a Mika, Samiri.
25 Mbale wa Mika, Isiya; a ana a Isiya, Zekariya,